Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb21 November tsamba 7
  • Mfundo Zothandiza Kuti Msonkhano Wokonzekera Utumiki Uzikhala Wabwino

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Mfundo Zothandiza Kuti Msonkhano Wokonzekera Utumiki Uzikhala Wabwino
  • Kabuku ka Msonkhano wa Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2021
  • Nkhani Yofanana
  • Mungatani Kuti Msonkhano Wokonzekera Utumiki Uzikhala Wothandiza?
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2015
  • Pindulani Mokwanira ndi Misonkhano Yokonzekera Utumiki wa Kumunda
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2006
  • Bokosi la Mafunso
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2001
  • Misonkhano Yokonzekera Utumiki Wakumunda
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2009
Onani Zambiri
Kabuku ka Msonkhano wa Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2021
mwb21 November tsamba 7
Zithunzi: 1. M’bale akukonzekera kuti akachititse msonkhano wokonzekera utumiki. Tizithunzi tosiyanasiyana tikuonetsa timapepala, munthu akuwerenga nkhani komanso mwininyumba akukana kulandira kapepala. 2. Tsiku lotsatira, m’bale uja akuchititsa msonkhano wokonzekera utumiki ndipo wanyamula kapepala komanso Baibulo.

MOYO WATHU WACHIKHRISTU

Mfundo Zothandiza Kuti Msonkhano Wokonzekera Utumiki Uzikhala Wabwino

Mofanana ndi mmene zilili ndi misonkhano ina yonse yampingo, misonkhano yokonzekera utumiki ndi mphatso yochokera kwa Yehova ndipo imatipatsa mwayi woti tilimbikitsane pa chikondi ndi ntchito zabwino. (Ahe 10:24, 25) Misonkhanoyi iyenera kuchitika kwa maminitsi 5 mpaka 7, ndipo nthawi imeneyi ikamatha, anthu ayenera kukhala atauzidwa kale oyenda naye, gawo lomwe akalalikire komanso pemphero laperekedwa. (Ngati msonkhanowu ukuchitika pambuyo pa msonkhano wina wa mpingo, uyenera kukhala waufupi kuposa pamenepa.) Wochititsa msonkhanowu ayenera kukonzekera bwino zinthu zomwe zingathandize amene akulowa mu utumiki patsikulo. Mwachitsanzo ngati ndi Loweruka, pamene anthu ambiri omwe abwera pamsonkhanowo ndi oti sanalowe mu utumiki kwa mlungu wonse, zingakhale zothandiza kungokambirana zomwe munganene polalikira. Kodi ndi nkhani zina ziti zimene mungakambirane pamsonkhanowu?

  • Chitsanzo cha zimene tinganene chopezeka mu Kabuku ka Msonkhano wa Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu

  • Mmene tingagwiritsire ntchito zochitika za posachedwapa poyamba kukambirana ndi anthu

  • Mmene tingayankhire munthu amene wanena zinthu zomwe anthu amakonda kunena ngati sakufuna kuti tikambirane nawo

  • Mmene tingayankhire munthu wokana Mulungu, wokhulupirira kuti zamoyo zinachita kusintha, wolankhula chinenero china kapena wa m’chipembedzo chimene si chofala m’dera lanu

  • Mmene tingagwiritsire ntchito webusaiti ya jw.org, JW Library® kapena Baibulo

  • Mmene tingagwiritsire ntchito chimodzi mwa zinthu zopezeka pa Zinthu Zophunzitsira

  • Mmene tingachitire mtundu winawake wa ulaliki monga kulalikira patelefoni, kulemba makalata, kulalikira m’malo opezeka anthu ambiri, kuchita maulendo obwereza kapena kuchititsa maphunziro a Baibulo

  • Kukumbutsana zofunikira pa nkhani ya kukhala otetezeka, kusintha mogwirizana ndi zomwe zikuchitika, kukhala ndi makhalidwe abwino, kuona zinthu moyenera, kapena mfundo zina zotero

  • Kukambirana phunziro kapena vidiyo ya m’kabuku ka Kuwerenga Komanso Kuphunzitsa Mwaluso

  • Mmene mungalimbikitsire kapena kuthandizira mnzanu amene mwayenda naye mu utumiki

  • Lemba logwirizana ndi utumiki kapena chitsanzo cholimbikitsa cha zimene zinachitikira ena mu utumiki

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena