Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb22 January tsamba 16
  • Muzithandiza Ophunzira Baibulo Kuti Asamacheze ndi Anthu Olakwika

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Muzithandiza Ophunzira Baibulo Kuti Asamacheze ndi Anthu Olakwika
  • Kabuku ka Msonkhano wa Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2022
  • Nkhani Yofanana
  • Muzithandiza Ophunzira Baibulo Kuti Asiye Makhalidwe Oipa
    Kabuku ka Msonkhano wa Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2022
  • Muzithandiza Ophunzira Anu Kuti Akhale pa Ubwenzi ndi Yehova
    Kabuku ka Msonkhano wa Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2022
  • Muzithandiza Ophunzira Baibulo Anu Kuti Azipezeka Pamisonkhano
    Kabuku ka Msonkhano wa Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2022
  • Muzilola Kuti Yehova Azikuthandizani Kudzera M’pemphero
    Kabuku ka Msonkhano wa Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2021
Onani Zambiri
Kabuku ka Msonkhano wa Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2022
mwb22 January tsamba 16

KUPHUNZITSA MWALUSO MU UTUMIKI | ZIMENE MUNGACHITE KUTI MUZISANGALALA KWAMBIRI MU UTUMIKI

Muzithandiza Ophunzira Baibulo Kuti Asamacheze ndi Anthu Olakwika

Kuti ophunzira Baibulo akhale pa ubwenzi wabwino ndi Yehova, ayenera kumacheza ndi anthu abwino. (Sl 15:1, 4) Anzawo abwino adzawathandiza kuti azichita zinthu zabwino.​—Miy 13:20; lff phunziro 48.

Muzikhala achifundo mukamathandiza ophunzira Baibulo anu kuti asamacheze ndi anthu a makhalidwe oipa. Zikhoza kuwavuta kuti asiye kucheza ndi anzawo amene ankacheza nawo poyamba. Choncho muzisonyeza kuti mumawaganizira ngakhale pa masiku amene simukuphunzira nawo. Mukhoza kuwatumizira meseji, kuwaimbira foni kapena kuwayendera kumene. Ophunzira Baibulo anu akamapita patsogolo, mungawaitane kuti mudzacheze nawo limodzi ndi abale ndi alongo ena. Mukamachita zimenezi, adzaona mosavuta kuti akupeza zambiri kuposa zimene akusiya. (Mko 10:29, 30) Inunso mudzasangalala kwambiri mukadzaona kuti banja la Yehova likukula.

ONERANI VIDIYO YAKUTI MUZITHANDIZA AMENE MUKUPHUNZIRA NAWO BAIBULO KUTI ASAMACHEZE NDI ANTHU OLAKWIKA, KENAKO YANKHANI MAFUNSO OTSATIRAWA:

  • Kodi kugwirizana ndi anthu oipa kumatanthauza chiyani?​—1Ak 15:33

  • Kodi Jane anaganiza kuti macheza Achikhristu angakhale otani?

  • Kodi Anita anamuthandiza bwanji Jane kuti asamacheze ndi anthu a makhalidwe oipa?

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena