Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • ijwwd nkhani 1
  • Kaulukidwe Kodabwitsa ka Ntchentche

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kaulukidwe Kodabwitsa ka Ntchentche
  • Kodi Zinangochitika Zokha?
  • Nkhani Yofanana
  • Ntchentche ya Kambalame—Ndi Tsoka la Afirika Kodi?
    Galamukani!—1996
  • Timapiko ta Ntchentche
    Galamukani!—2012
  • Ntchentche Zonyansazo—kodi Zili Ndi Ntchito Imene Simumaganizirapo?
    Galamukani!—1996
  • Musawaope
    Imbirani Yehova Mosangalala
Onani Zambiri
Kodi Zinangochitika Zokha?
ijwwd nkhani 1
Ntchentche

KODI ZINANGOCHITIKA ZOKHA?

Kaulukidwe Kodabwitsa ka Ntchentche

Munthu aliyense amene wayesapo kupha ntchentche amadziwa kuti ndi zovuta kwambiri. Zili choncho chifukwa zimathawa mwamsanga.

Asayansi apeza kuti ntchentche zamtundu winawake zimatha kutembenuka mofanana ndi ndege zankhondo ndipo zimachita zimenezi sekondi imodzi isanathe. Pulofesa wina dzina lake Michael Dickinson ananena kuti ntchentchezi “zikangobadwa kumene zimatha kuuluka mwaukatswiri kwambiri. Zimakhala ngati kakhanda kamene kamabadwa kakudziwa kale kuyendetsa ndege yankhondo.”

Ochita kafukufuku anajambula ntchentchezi zikuuluka ndipo anapeza kuti zimakupiza mapiko awo maulendo 200 pa sekondi iliyonse. Koma zikangokupiza kamodzi zimatha kutembenuka n’kuyamba kuthawa.

Ochita kafukufuku apezanso kuti nthawi imene ntchentchezi zimatenga kuchokera pamene zaona zoopsa kufika poti zithawe ndi yochepa kwambiri moti zingachitike maulendo 50 munthu asanamalize kuphethira. Dickinson ananenanso kuti: “M’kanthawi kochepa kwambiri, ntchentche zimenezi zimazindikira kumene kuli zoopsa n’kudziwa koyenera kuthawira.”

Akatswiri amafunitsitsa kudziwa mmene kaubongo ka ntchentchezi kamachitira zimenezi.

Ntchentche ikuuluka n’kumatembenuka

Ntchentchezi zimatha kutembenuka sekondi imodzi isanathe n’kuyamba kuthawa

Kodi inuyo mukuganiza bwanji? Kodi zinangochitika zokha kuti ntchentche zamtunduwu zikhale ndi luso limeneli? Kapena kodi ntchentchezi zinachita kulengedwa?

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena