Mawu a M'munsi
b Mungaone zithunzi za zidutswa zotchedwa P. Fouad Inv. No. 266 za Deuteronomo wa mumpukutu wa Baibulo la LXX, pa mas. 1940, 1941. Zidutswa 12 zimenezi tazipatsa manambala. Zidutswazi zili ndi zilembo zinayi zoimira dzina la Mulungu zimene azizunguliza ndi mzere. Zina mwa izo zili ndi zilembo zoimira dzina la Mulungu m’malo oposa amodzi. Na. 1, chithunzi cha Deuteronomo 31:28 mpaka 32:7, chikusonyeza zilembo zinayi zoimira dzina la Mulungu pamzere wa 7 ndi wa 15. Na. 2 (De 31:29, 30) zilembozi zili pamzere wa 6. Na. 3 (De 20:12-14, 17-19) pamzere wachitatu ndi wa 7. Na. 4 (De 31:26) pamzere woyamba. Na. 5 (De 31:27, 28) pamzere wachisanu. Na. 6 (De 27:1-3) pamzere wachisanu. Na. 7 (De 25:15-17) pamzere wachitatu. Na. 8 (De 24:4) pamzere wachisanu. Na. 9 (De 24:8-10) pamzere wachitatu. Na. 10 (De 26:2, 3) pamzere woyamba. Na. 11 mbali ziwiri (De 18:4-6) pamzere wachisanu ndi wa 6, ndipo Na. 12 (De 18:15, 16) pamzere wachitatu.