Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 12/94 tsamba 2
  • Kodi Nthaŵi Yanu ya Kusonkhana Idzasintha?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Nthaŵi Yanu ya Kusonkhana Idzasintha?
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—1994
  • Nkhani Yofanana
  • Lingalirani za Ena—mbali 1
    Utumiki Wathu wa Ufumu—1995
  • Ndandanda Yatsopano ya Misonkhano ya Mpingo
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2008
  • Misonkhano Imene Imatilimbikitsa “pa Chikondi Ndi Ntchito Zabwino”
    Gulu Lochita Chifuniro cha Mulungu
  • Kusonkhana Kuti Tilambire Mulungu
    Ufumu wa Mulungu Ukulamulira
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—1994
km 12/94 tsamba 2

Kodi Nthaŵi Yanu ya Kusonkhana Idzasintha?

Ngati mipingo ingapo imene imagwiritsira ntchito Nyumba Yaufumu imodzi yamvana kumasinthana kapena kusintha nthaŵi ya kusonkhana, chimenechi chiyenera kuchitidwa pa 1 January. Kukhala ofunitsitsa kugwirizana ndi makonzedwe amene akhazikitsidwa kumasonyeza kukondana ndi kulingalirana. Kaŵirikaŵiri kusintha kwa nthaŵi ya kusonkhana kudzakhala bwino kumbali yanu, kukumachititsa kupezeka pamisonkhano kukhala kosavuta.

Komano, mwinamwake kusintha kumene kukuchitika chaka chino sikungayenerane bwino ndi programu ya zochita zanu. Mungafunikire kupanga masinthidwe pa zochita zanu amene mwina sangakukhalireni bwino kwenikweni. Kufunitsitsa kwa aliyense kugwirizana kumasonyeza kuyamikira makonzedwe onse, kumene kumapindulitsa aliyense woloŵetsedwamo.

Indedi, kusinthana nthaŵi ya kusonkhana kotsatira kungadzakuyendereni bwino. Pakali pano, mukulimbikitsidwa kupanga masinthidwe aumwini ofunika kotero kuti mukhale wokhoza kumapezeka pamisonkhano yonse ya mlungu ndi mlungu malinga ndi ndandanda imene yasankhidwa ndi mpingo. Yesayesani kukhala ndi kaonedwe ka wamasalmo Davide, yemwe analengeza kuti: “Ndinakondwera mmene ananena nane, Tiyeni ku nyumba ya Yehova.”—Sal. 122:1.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena