Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 12/99 tsamba 7
  • Sukulu ya Utumiki Wateokalase ya 2000

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Sukulu ya Utumiki Wateokalase ya 2000
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—1999
  • Nkhani Yofanana
  • Sukulu ya Utumiki Wateokalase ya 2001
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2000
  • Sukulu Yautumiki Wateokratiki ya 1998
    Utumiki Wathu wa Ufumu—1997
  • Sukulu ya Utumiki Wateokalase Imapindulitsa
    Buku Lolangiza la Sukulu ya Utumiki Wateokalase
  • Sukulu Imene Imatikonzekeretsa Kuchita Zinthu Zimene Zili Zofunika Kwambiri
    Utumiki wathu wa Ufumu—2002
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—1999
km 12/99 tsamba 7

Sukulu ya Utumiki Wateokalase ya 2000

1 Kwa anthu a Yehova, Sukulu ya Utumiki Wateokalase yakhala dalitso kwambiri. Kwa zaka zoposa 50 zapitazi, yathandiza mamiliyoni a anthu kukulitsa maluso awo monga okamba nkhani poyera ndi aphunzitsi a choonadi cha Baibulo. (Sal. 145:10-12; Mat. 28:19, 20) Kodi mungaone mmene sukulu yakuthandizirani? Ingapitirize kutero m’chaka cha 2000 ngati mutengamo mbali mokwanira ndi kugwiritsira ntchito uphungu woperekedwawo.

2 Malangizo a nkhani ndi zofalitsa zimene zidzagwiritsidwa ntchito zalembedwa patsamba loyamba la ndandanda ya sukulu ya 2000. Nthaŵi ya nkhani iliyonse, komwe yatengedwa, mmene iyenera kuperekedwera, ndi nkhani zina zaperekedwa. Chonde khalani ndi nthaŵi yoŵerenga malangizoŵa bwinobwino ndi kuwagwiritsira ntchito.

3 Kuŵerenga Baibulo Mlungu ndi Mlungu: Pa ndandanda ya sukulu pali mbali ziŵiri zosiyana za kuŵerenga Baibulo mlungu ndi mlungu. Imodzi ndi muyeso wa nkhani yoŵerenga Baibulo imene utali wake umakhala pafupifupi masamba asanu a Baibulo. Mfundo za Baibulo zimachokera pa kuŵerenga kumeneku. Kuŵerenga kwinako ndi kowonjezera kumene kumakhala kotalikirapo kuŵirikiza kaŵiri koyambako. Mwakutsatira zimenezi, mukhoza kumaliza kuŵerenga Baibulo lonse m’zaka zitatu. N’kodziŵikiratu kuti ena angafune kuŵerenga kuposa mmene zaikidwira m’mbali yowonjezeredwayi, ndipo ena sangakwanitse kuyendera nayo limodzi. M’malo modziyerekezera ndi ena, kondwerani ndi zimene mungakwaniritse. (Agal. 6:4) Chofunika kwambiri n’kuŵerenga Mawu a Mulungu tsiku lililonse.—Sal. 1:1-3.

4 Kuti mulembetse m’Sukulu ya Utumiki Wateokalase, lankhulani ndi woyang’anira sukulu. Musaone nkhani imene mwapatsidwa mwachibwanabwana, ndipo musalephere wambawamba kuikamba. Itengeni sukuluyi monga makonzedwe ochokera kwa Yehova. Konzekerani bwino, khalani ozoloŵerana ndi nkhani imene mwapatsidwa, ndipo lankhulani kuchokera pansi pa mtima, motero mukumapindula kwambiri ndi sukulu yapaderayi.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena