25 Koma pa tsiku lachitatu, pamene anthuwo anali pa ululu,+ ana awiri a Yakobo, Simiyoni ndi Levi,+ alongo ake a Dina,+ aliyense anatenga lupanga lake n’kukalowa mumzindawo mosaonetsera cholinga chawo. Kenako anayamba kupha mwamuna aliyense.+
16 Awa ndi mayina a ana aamuna a Levi,+ malinga ndi mzere wobadwira wa makolo awo:+ Gerisoni, Kohati ndi Merari.+ Ndipo Levi anakhala ndi moyo zaka 137.