Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • 1 Mafumu 13:2
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 2 Ndiyeno anafuulira guwa lansembelo mawu ochokera kwa Yehova oitanira tsoka, kuti: “Guwa lansembe iwe! Guwa lansembe iwe! Yehova wanena kuti, ‘Mwana wamwamuna adzabadwa m’nyumba ya Davide, dzina lake Yosiya.+ Ndithu adzatenga ansembe a malo okwezeka amene akufukiza nsembe yautsi pa iwe, n’kuwapereka nsembe pa iwe. Iye adzawotcha mafupa a anthu pa iwe.’”+

  • 2 Mafumu 23:8
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 8 Kenako inaitanitsa ansembe onse kuchokera m’mizinda ya Yuda. Inawaitanitsa kuti isandutse malo okwezeka kukhala osayenera kulambirako, kumene ansembewo ankafukizako nsembe yautsi, kuyambira ku Geba+ mpaka ku Beere-seba.+ Inagwetsa malo okwezeka a pazipata amene anali pakhomo la pachipata cha Yoswa mkulu wa mzindawo. Chipata cha Yoswacho chinali mbali ya kumanzere munthu akamalowa pachipata cha mzindawo.

  • 2 Mbiri 34:3
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 3 M’chaka cha 8 cha ulamuliro wa Yosiya, iye akadali mnyamata,+ anayamba kufunafuna+ Mulungu wa Davide kholo lake. M’chaka cha 12 anayamba kuyeretsa+ Yuda ndi Yerusalemu pochotsa malo okwezeka,+ mizati yopatulika,+ zifaniziro zogoba,+ ndi zifaniziro zopangidwa ndi zitsulo zosungunula.

  • Yesaya 27:9
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 9 Chotero zolakwa za Yakobo zidzaphimbidwa mwa njira imeneyi.+ Zimenezi zidzachitika akadzachotsa tchimo lakelo,+ ndiponso akadzasandutsa miyala yonse ya paguwa lansembe kukhala miyala yofewa kwambiri yonyenyekanyenyeka, moti mizati yopatulika+ ndi maguwa ofukizirapo zonunkhira sizidzamangidwanso.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena