3Tsopano Mose anakhala m’busa wa ziweto za Yetero,*+ wansembe wa ku Midiyani, amene anali apongozi ake.+ Pamene anali kuweta ziwetozo chakumadzulo kwa chipululu, anafika kuphiri la Mulungu woona,+ ku Horebe.+
1Yehova anapitiriza kulankhula ndi Mose m’chipululu cha Sinai,+ m’chihema chokumanako.+ Analankhula naye pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri m’chaka chachiwiri, atatuluka m’dziko la Iguputo.+ Iye anati: