24 Koma mtumiki wanga Kalebe,+ chifukwa wasonyeza kuti ali ndi mzimu wosiyana ndi wa ena, ndipo wakhala akunditsatira ndi mtima wonse,+ ndithudi ndidzam’lowetsa m’dziko limene anakalizonda, ndipo mbadwa zake zidzakhalamo ngati dziko lawo.+
17 Komanso, adzatsogola monga kalambulabwalo wa Mulungu ali ndi mzimu ndi mphamvu ngati za Eliya.+ Iye adzatembenuza mitima+ ya abambo kuti ikhale ngati ya ana, ndipo osamvera adzawatembenuzira ku nzeru yeniyeni ya anthu olungama. Adzachita izi kuti asonkhanitsire Yehova+ anthu okonzedwa.”+