13 Hafu ya fuko la Manase ndinalipatsa dera lotsala la Giliyadi+ ndi Basana+ yense wa ufumu wa Ogi. Kodi si paja dera lonse la Arigobi+ limene ndi Basana yense, limatchedwa dziko la Arefai?+
31 Mose anapereka hafu ya dera la Giliyadi, Asitaroti,+ Edirei,+ ndi mizinda ya ufumu wa Ogi m’dziko la Basana kwa ana a Makiri,+ mwana wa Manase. Anapereka dzikoli kwa hafu ya ana a Makiri potsata mabanja awo.
17Fuko la Manase, mwana woyamba wa Yosefe,+ linapatsidwa gawo lake.+ Makiri+ mwana woyamba wa Manase,+ bambo wake wa Giliyadi,+ anali mwamuna wamphamvu pankhondo,+ ndipo gawo lake linali Giliyadi+ ndi Basana.