19 ndipo uyandikire pafupi ndi ana a Amoni. Usawavutitse kapena kumenyana nawo, chifukwa sindidzakupatsa mbali iliyonse ya dziko la ana a Amoni kuti likhale lako. Dziko limeneli ndinalipereka kwa ana a Loti kuti likhale lawo.+
37 Koma simunayandikire dziko la ana a Amoni,+ dera lonse la m’mbali mwa chigwa cha Yaboki,+ kapena mizinda ya m’dera lamapiri, kapenanso malo alionse amene Yehova Mulungu wathu sanatilamule kuti tiwalande.
10 Tsopano taonani zimene akuchita ana a Amoni,+ ana a Mowabu+ ndi a kudera lamapiri la Seiri.+ Inu simunalole kuti Aisiraeli alowe m’dziko lawo pamene anali kutuluka m’dziko la Iguputo ndipo anawasiya osawawononga.+