5 koma mudzafunefune malo amene Yehova Mulungu wanu adzasankhe pakati pa mafuko anu onse kuti aikepo dzina lake, kuti lizikhala pamenepo. Amenewo ndiwo malo amene muzidzapitako.+
19 Pamapeto pake anati: “Pajatu ku Silo+ kumachitika chikondwerero cha Yehova chaka ndi chaka. Mzinda wa Silo uli kum’mwera kwa Beteli, chakum’mawa kwa msewu waukulu wochokera ku Beteli kupita ku Sekemu,+ ndiponso chakum’mwera kwa Lebona.”