11 Inu Yehova, ukulu,+ mphamvu,+ kukongola,+ ulemerero,+ ndi ulemu+ ndi zanu, chifukwa zinthu zonse zakumwamba ndi za padziko lapansi ndi zanu.+ Ufumu+ ndi wanu, inu Yehova, ndinunso Wokwezeka monga mutu pa onse.+
3 Pakuti ine ndine Yehova Mulungu wako, Woyera wa Isiraeli ndiponso Mpulumutsi wako.+ Ndapereka Iguputo monga dipo* lokuwombolera.+ Ndaperekanso Itiyopiya+ ndi Seba m’malo mwako.