7 Koma Yehova anauza Samueli kuti: “Usaone maonekedwe ake ndi kutalika kwa msinkhu wake,+ pakuti ine ndamukana ameneyu. Chifukwa mmene munthu amaonera si mmene Mulungu amaonera.+ Munthu amaona zooneka ndi maso,+ koma Yehova amaona mmene mtima ulili.”+
30 inuyo mumve muli kumwamba, malo anu okhala okhazikika,+ ndipo mukhululuke+ ndi kuchitapo kanthu. Mupatse aliyense malinga ndi njira zake zonse,+ popeza mukudziwa mtima wake+ (popeza inu nokha ndiye mumadziwa bwino mtima wa ana a anthu).+