-
2 Mbiri 8:14Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
14 Kuwonjezera pamenepo, Solomo anaika magulu+ a ansembe pa utumiki wawo mogwirizana ndi lamulo la Davide bambo ake.+ Anaikanso Alevi+ pamalo awo a ntchito kuti azitamanda+ ndi kutumikira+ pamaso pa ansembe mogwirizana ndi dongosolo la tsiku ndi tsiku.+ Komanso anaika alonda a pazipata m’magulu awo kuti akhale m’zipata zosiyanasiyana+ chifukwa ndilo linali lamulo la Davide munthu wa Mulungu woona.
-
-
2 Mbiri 31:2Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
2 Kenako Hezekiya anaika magulu+ a ansembe ndi Alevi+ mogwirizana ndi magulu awo. Gulu lililonse analiika mogwirizana ndi utumiki wawo monga ansembe+ ndi Alevi+ ogwira ntchito yokhudza nsembe yopsereza+ ndi nsembe zachiyanjano.+ Anawaika m’maguluwa kuti azitumikira,+ kuyamika+ ndi kutamanda+ Mulungu m’zipata za kachisi wa Yehova.
-