Deuteronomo 33:2 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 2 Ndipo anati:“Yehova anafika kuchokera ku Sinai,+Anathwanima pa iwo kuchokera ku Seiri.+Anawala kuchokera kudera lamapiri la Parana,+Ndipo anali ndi miyandamiyanda ya oyera ake,+Kudzanja lake lamanja kunali ankhondo ake.+ 2 Mafumu 6:17 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 17 Kenako Elisa anayamba kupemphera+ kuti: “Inu Yehova, m’tseguleni maso+ chonde kuti aone.” Nthawi yomweyo Yehova anatsegula maso a mtumiki uja, moti anaona kuti dera lonse lamapiri kuzungulira Elisa+ linadzaza ndi mahatchi ndi magaleta ankhondo+ oyaka moto. Danieli 7:10 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 10 Mtsinje wa moto unali kuyenda kuchokera kwa iye.+ Panali atumiki okwana miliyoni imodzi amene anali kumutumikira nthawi zonse,+ ndi atumiki enanso mamiliyoni 100 amene anali kuimirira pamaso pake nthawi zonse.+ Bwalo la milandu+ linakhala pansi, ndipo mabuku anatsegulidwa. Mateyu 26:53 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 53 Kapena ukuganiza kuti sindingapemphe Atate wanga kuti anditumizire magulu ankhondo oposa 12 a angelo nthawi yomwe ino?+ Chivumbulutso 5:11 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 11 Kenako, ndinaona ndi kumva mawu a angelo ambiri atazungulira mpando wachifumu limodzi ndi zamoyo zija ndi akulu aja. Chiwerengero chawo chinali miyanda kuchulukitsa ndi miyanda*+ ndiponso masauzande kuchulukitsa ndi masauzande.+
2 Ndipo anati:“Yehova anafika kuchokera ku Sinai,+Anathwanima pa iwo kuchokera ku Seiri.+Anawala kuchokera kudera lamapiri la Parana,+Ndipo anali ndi miyandamiyanda ya oyera ake,+Kudzanja lake lamanja kunali ankhondo ake.+
17 Kenako Elisa anayamba kupemphera+ kuti: “Inu Yehova, m’tseguleni maso+ chonde kuti aone.” Nthawi yomweyo Yehova anatsegula maso a mtumiki uja, moti anaona kuti dera lonse lamapiri kuzungulira Elisa+ linadzaza ndi mahatchi ndi magaleta ankhondo+ oyaka moto.
10 Mtsinje wa moto unali kuyenda kuchokera kwa iye.+ Panali atumiki okwana miliyoni imodzi amene anali kumutumikira nthawi zonse,+ ndi atumiki enanso mamiliyoni 100 amene anali kuimirira pamaso pake nthawi zonse.+ Bwalo la milandu+ linakhala pansi, ndipo mabuku anatsegulidwa.
53 Kapena ukuganiza kuti sindingapemphe Atate wanga kuti anditumizire magulu ankhondo oposa 12 a angelo nthawi yomwe ino?+
11 Kenako, ndinaona ndi kumva mawu a angelo ambiri atazungulira mpando wachifumu limodzi ndi zamoyo zija ndi akulu aja. Chiwerengero chawo chinali miyanda kuchulukitsa ndi miyanda*+ ndiponso masauzande kuchulukitsa ndi masauzande.+