9 Tsopano anandiuza kuti: “Losera kwa mphepo. Iwe mwana wa munthu, losera ndipo uuze mphepoyo kuti, ‘Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti: “Iwe mphepo! Bwera kuchokera kumbali zonse zinayi ndi kuwomba anthu ophedwawa+ kuti akhalenso ndi moyo.”’”+