3 Aliyense amene ali pakati panu mwa anthu onse amene amamutumikira, Mulungu wake akhale naye.+ Choncho apite ku Yerusalemu m’dziko la Yuda n’kukamanganso nyumba ya Yehova Mulungu wa Isiraeli, yomwe inali ku Yerusalemu.+ Iye ndiye Mulungu woona.+
11 Koma inu anthu a ku Yuda, nthawi yoti musonkhanitsidwe ngati pa nthawi yokolola yakhazikitsidwa. Ine ndidzasonkhanitsanso anthu anga amene anagwidwa ndi kutengedwa kupita kudziko lina.”+