Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Genesis 13:10
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 10 Choncho, Loti anakweza maso ake n’kuona Chigawo* chonse cha Yorodano+ mpaka kukafika ku Zowari,+ ndipo anaona kuti chinali chigawo chobiriwira bwino. Chinali chobiriwira bwino kwambiri ngati mmene unalili munda wa Yehova+ komanso ngati mmene linalili dziko la Iguputo. Pa nthawiyi n’kuti Yehova asanawononge Sodomu ndi Gomora.

  • Yesaya 35:1
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 35 Chipululu ndi malo opanda madzi zidzasangalala.+ Dera lachipululu lidzakondwa ndipo lidzachita maluwa n’kukhala lokongola ngati duwa la safironi.+

  • Yesaya 41:18
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 18 Ndidzatsegula mitsinje pamapiri opanda zomera zilizonse, ndipo pakatikati pa zigwa ndidzatsegulapo akasupe.+ Chipululu ndidzachisandutsa dambo lamadzi, ndipo dziko lopanda madzi ndidzalisandutsa pochokera madzi.+

  • Ezekieli 31:8
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 8 Mitengo ina ya mkungudza sinafanane ndi mtengo umenewu m’munda wa Mulungu.+ Nthambi zikuluzikulu za mitengo ina yooneka ngati mkungudza, sizinafanane ndi za mtengo umenewu. Nthambi za mitengo ya katungulume sizinafanane ndi nthambi za mtengo umenewu. Panalibenso mtengo wina m’munda wa Mulungu umene unali wokongola ngati mtengo umenewu.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena