2 Deralo lidzachitadi maluwa.+ Lidzasangalala ndipo lidzakondwera n’kufuula ndi chisangalalo.+ Lidzapatsidwa ulemerero wa Lebanoni+ ndi kukongola kwa Karimeli+ ndiponso kwa Sharoni.+ Padzakhala anthu amene adzaone ulemerero wa Yehova+ ndi kukongola kwa Mulungu wathu.+
19 M’chipululu ndidzabzalamo mtengo wa mkungudza, mtengo wa mthethe, mtengo wa mchisu, ndi mtengo wamafuta.+ M’dera lachipululu ndidzabzalamo mtengo wofanana ndi mkungudza, mtengo wa ashi,* ndi mtengo wa paini pa nthawi imodzimodziyo.+