Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Deuteronomo 30:3
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 3 Yehova Mulungu wanu adzabweza kwawo anthu a mtundu wanu amene anagwidwa ndi kupita kudziko lina,+ ndipo adzakumverani chifundo+ n’kukusonkhanitsaninso pamodzi kuchokera pakati pa anthu onse kumene Yehova Mulungu wanu anakubalalitsirani.+

  • Yesaya 11:16
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 16 Padzakhala msewu waukulu+ wochokera kudziko la Asuri woti mudzadutse anthu ake amene adzatsale,+ monga mmene panalili msewu umodzi umene Aisiraeli anayendamo m’tsiku limene anatuluka m’dziko la Iguputo.

  • Yesaya 43:6
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 6 Ndidzauza kumpoto kuti,+ ‘Abwezere kwawo!’ ndipo ndidzauza kum’mwera kuti, ‘Usawakanize! Bweretsa ana anga aamuna kuchokera kutali, ndi ana anga aakazi kuchokera kumalekezero a dziko lapansi.+

  • Yesaya 54:3
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 3 Pakuti iwe udzafutukukira mbali ya kudzanja lamanja ndi kumanzere, ndipo ana ako+ adzalanda ngakhale mitundu ya anthu.+ Iwo adzakhala m’mizinda imene inasiyidwa yabwinja.+

  • Yesaya 60:4
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 4 “Takweza maso ako uone zonse zimene zikuchitika mokuzungulira. Onse asonkhanitsidwa pamodzi.+ Abwera kwa iwe.+ Kuchokera kutali, ana ako aamuna akubwera limodzi ndi ana ako aakazi, amene adzasamalidwe atanyamulidwa m’manja.+

  • Mateyu 24:31
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 31 Iye adzatumiza angelo ake ndi kulira kwamphamvu kwa lipenga,+ ndipo adzasonkhanitsa osankhidwa ake+ kuchokera kumphepo zinayi,+ kuchokera kumalekezero a m’mlengalenga mpaka kumalekezero ena.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena