-
Ezekieli 25:3Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
3 Uuze ana a Amoniwo kuti, ‘Imvani mawu a Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa. Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti: “Chifukwa chakuti malo anga opatulika adetsedwa, inu mwanena kuti: Eyaa! Zakhala bwino! Mwaneneranso zimenezi dziko la Isiraeli chifukwa chakuti lakhala bwinja, komanso nyumba ya Yuda chifukwa chakuti anthu ake atengedwa ukapolo.+
-
-
Ezekieli 29:3Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
3 Unene kuti, ‘Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti: “Ine ndilanga iwe Farao mfumu ya Iguputo.+ Ndiwe chilombo chachikulu cha m’nyanja+ chimene chagona m’ngalande zake zotuluka mumtsinje wa Nailo.+ Ndiwe chilombo chimene chanena kuti, ‘Mtsinje wa Nailo ndi wanga, ndipo ineyo ndinaupanga ndekha.’+
-