2 Mbiri 36:16 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 16 Koma iwo ankangonyogodola+ amithenga a Mulungu woona, kunyoza mawu ake+ ndi kuseka+ aneneri ake, mpaka kufika poti panalibenso chiyembekezo choti angathe kuchiritsidwa.+ Kenako mkwiyo+ wa Yehova unawagwera. Salimo 2:9 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 9 Mitunduyo udzaiswa ndi ndodo yachifumu yachitsulo,+Udzaiphwanya ngati mbiya yadothi, n’kukhala zidutswazidutswa.”+ Yesaya 30:14 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 14 Munthu adzaugwetsa ngati mmene amaphwanyira mtsuko waukulu wadothi,+ mtsukowo n’kuphwanyikiratu wonse n’kungokhala tizidutswatizidutswa, ndipo patizidutswapo osapezeka ngakhale phale loti n’kupalira moto kapena kutungira madzi padambo.”+ Maliro 4:2 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 2 Ana okondedwa a Ziyoni+ amene anali amtengo wapatali ngati golide woyengeka bwino,Tsopano ayamba kuonedwa ngati mitsuko ikuluikulu yadothi, ntchito ya manja a munthu woumba mbiya.+ Chivumbulutso 2:27 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 27 Iyeyo adzakusa anthu ndi ndodo yachitsulo,+ ngati imenenso ine ndailandira kwa Atate wanga. Anthuwo adzaphwanyidwaphwanyidwa ngati mbiya zadothi.+
16 Koma iwo ankangonyogodola+ amithenga a Mulungu woona, kunyoza mawu ake+ ndi kuseka+ aneneri ake, mpaka kufika poti panalibenso chiyembekezo choti angathe kuchiritsidwa.+ Kenako mkwiyo+ wa Yehova unawagwera.
9 Mitunduyo udzaiswa ndi ndodo yachifumu yachitsulo,+Udzaiphwanya ngati mbiya yadothi, n’kukhala zidutswazidutswa.”+
14 Munthu adzaugwetsa ngati mmene amaphwanyira mtsuko waukulu wadothi,+ mtsukowo n’kuphwanyikiratu wonse n’kungokhala tizidutswatizidutswa, ndipo patizidutswapo osapezeka ngakhale phale loti n’kupalira moto kapena kutungira madzi padambo.”+
2 Ana okondedwa a Ziyoni+ amene anali amtengo wapatali ngati golide woyengeka bwino,Tsopano ayamba kuonedwa ngati mitsuko ikuluikulu yadothi, ntchito ya manja a munthu woumba mbiya.+
27 Iyeyo adzakusa anthu ndi ndodo yachitsulo,+ ngati imenenso ine ndailandira kwa Atate wanga. Anthuwo adzaphwanyidwaphwanyidwa ngati mbiya zadothi.+