5 “Yehova wanena zimene zidzachitikire aneneri amene akusocheretsa anthu a mtundu wanga.+ Aneneri amenewo akutafuna chakudya ndi mano awo+ n’kumanena kuti, ‘Mtendere!’+ Koma munthu akapanda kuika chakudya m’kamwa mwawo, amakonzekera kumuthira nkhondo.+ Kwa iwo Mulungu wanena kuti,