20 “M’tsiku limenelo, pogwiritsira ntchito lezala lobwereka la kuchigawo cha ku Mtsinje,*+ pogwiritsira ntchito mfumu ya Asuri,+ Yehova adzameta tsitsi la kumutu ndi tsitsi la m’mapazi, ndipo lezalalo lidzachotseratu ngakhale ndevu.+
2 Iye wapita kukachisi ndi ku Diboni.+ Wapita kumalo okwezeka kukalira. Mowabu akulira mofuula chifukwa cha Nebo+ ndi Medeba.+ Anthu onse a mmenemo ameta mipala.+ Ndevu za munthu aliyense zametedwa.