Yesaya 21:9 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 9 Tsopano taonani! Kukubwera magaleta ankhondo okokedwa ndi mahatchi awiriawiri, mutakwera amuna ankhondo.”+ Kenako iye anayamba kufuula kuti: “Wagwa! Babulo wagwa!+ Zifaniziro zonse zogoba za milungu yake zaphwanyidwa ndipo zili pansi.”+ Yesaya 47:9 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 9 Koma zinthu ziwiri izi zidzakugwera modzidzimutsa tsiku limodzi:+ Ana ako adzafa ndiponso udzakhala wamasiye. Zimenezi zidzakugwera ndithu,+ chifukwa cha zamatsenga zochuluka zimene wachita, chifukwa cha kuchuluka kwa mphamvu zako zamatsenga, ndiponso chifukwa chakuti wazichita kwambiri.+ 1 Atesalonika 5:2 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 2 Pakuti inu eni mukudziwa bwino kuti tsiku la Yehova*+ lidzabwera ndendende ngati mbala usiku.+ Chivumbulutso 14:8 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 8 Kenako mngelo wina wachiwiri anamutsatira, ndipo anati: “Wagwa! Babulo+ Wamkulu wagwa,+ amene anachititsa mitundu yonse ya anthu kumwako vinyo+ wa mkwiyo wake ndi wa dama* lake!”+ Chivumbulutso 18:2 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 2 Iye anafuula ndi mawu amphamvu,+ akuti: “Wagwa! Babulo Wamkulu wagwa,+ ndipo wakhala malo okhala ziwanda, ndiponso obisalamo mpweya+ uliwonse wonyansa wotuluka m’kamwa, komanso obisalamo mbalame iliyonse yonyansa ndi yodedwa.+
9 Tsopano taonani! Kukubwera magaleta ankhondo okokedwa ndi mahatchi awiriawiri, mutakwera amuna ankhondo.”+ Kenako iye anayamba kufuula kuti: “Wagwa! Babulo wagwa!+ Zifaniziro zonse zogoba za milungu yake zaphwanyidwa ndipo zili pansi.”+
9 Koma zinthu ziwiri izi zidzakugwera modzidzimutsa tsiku limodzi:+ Ana ako adzafa ndiponso udzakhala wamasiye. Zimenezi zidzakugwera ndithu,+ chifukwa cha zamatsenga zochuluka zimene wachita, chifukwa cha kuchuluka kwa mphamvu zako zamatsenga, ndiponso chifukwa chakuti wazichita kwambiri.+
8 Kenako mngelo wina wachiwiri anamutsatira, ndipo anati: “Wagwa! Babulo+ Wamkulu wagwa,+ amene anachititsa mitundu yonse ya anthu kumwako vinyo+ wa mkwiyo wake ndi wa dama* lake!”+
2 Iye anafuula ndi mawu amphamvu,+ akuti: “Wagwa! Babulo Wamkulu wagwa,+ ndipo wakhala malo okhala ziwanda, ndiponso obisalamo mpweya+ uliwonse wonyansa wotuluka m’kamwa, komanso obisalamo mbalame iliyonse yonyansa ndi yodedwa.+