18 Mfumuyo inatenga ziwiya zonse,+ zazikulu+ ndi zazing’ono, za m’nyumba ya Mulungu woona. Inatenganso chuma+ cha m’nyumba ya Yehova, chuma cha mfumu+ ndi cha akalonga ake. Inatenga chilichonse n’kupita nacho ku Babulo.
17 “Isiraeli ndi nkhosa yosochera.+ Mikango ndi imene yamuchititsa kuthawa.+ Poyamba, mfumu ya Asuri inadya Isiraeli,+ ndipo ulendo uno Nebukadirezara mfumu ya ku Babulo yakukuta mafupa ake.+