16 Koma iwo ankangonyogodola+ amithenga a Mulungu woona, kunyoza mawu ake+ ndi kuseka+ aneneri ake, mpaka kufika poti panalibenso chiyembekezo choti angathe kuchiritsidwa.+ Kenako mkwiyo+ wa Yehova unawagwera.
8 Nthawi zonse ndikalankhula mawu anu ndimalira. Ndimanena za chiwawa ndi kufunkhidwa,+ pakuti mawu a Yehova achititsa kuti ndizinyozedwa ndi kutonzedwa tsiku lonse.+