19 Babulo, amene ndi chokongoletsera maufumu,+ chinthu chokongola ndi chonyadira cha Akasidi,+ adzakhala ngati pamene Mulungu anagonjetsa Sodomu ndi Gomora.+
14 Pakuti mitundu yambiri ndi mafumu otchuka+ agwiritsa ntchito anthu anga monga antchito awo.+ Chotero ndidzawabwezera mogwirizana ndi zochita zawo ndiponso mogwirizana ndi ntchito za manja awo.’”+