18 Ndikauza munthu woipa kuti, ‘Udzafa ndithu,’+ iwe osamulankhula munthu woipayo ndi kumuchenjeza kuti asiye njira yake yoipa n’cholinga choti akhalebe ndi moyo,+ iyeyo poti ndi woipa adzafa chifukwa cha zolakwa zake,+ koma magazi ake ndidzawafuna kuchokera m’manja mwako.+