29 Pakuti ndikudziwa bwino kuti pambuyo pa imfa yanga, mosakayikira mudzachita zinthu zokuwonongetsani+ ndipo mudzapatuka ndi kusiya njira imene ndakulamulani kuyendamo. Pamapeto pake tsoka+ lidzakugwerani, chifukwa mudzachita zoipa pamaso pa Yehova ndi kumulakwira ndi ntchito za manja anu.”+
14 Komanso, anthu ndi atsogoleri onse a ansembe+ anachita zosakhulupirika zochuluka kwambiri mofanana ndi zonyansa zonse+ za anthu a mitundu ina. Choncho iwo anaipitsa nyumba ya Yehova imene iye anaiyeretsa ku Yerusalemu.+