Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Deuteronomo 31:29
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 29 Pakuti ndikudziwa bwino kuti pambuyo pa imfa yanga, mosakayikira mudzachita zinthu zokuwonongetsani+ ndipo mudzapatuka ndi kusiya njira imene ndakulamulani kuyendamo. Pamapeto pake tsoka+ lidzakugwerani, chifukwa mudzachita zoipa pamaso pa Yehova ndi kumulakwira ndi ntchito za manja anu.”+

  • Deuteronomo 32:15
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 15 Yesuruni*+ atayamba kunenepa, anayamba kupanduka.+

      Iwe wanenepa, wakulupala, wakhuta mopitirira muyezo.+

      Pamenepo iye anasiya Mulungu amene anam’panga,+

      Ndi kunyoza Thanthwe+ la chipulumutso chake.

  • Yoswa 23:16
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 16 Adzatero chifukwa chakuti mwaphwanya pangano la Yehova Mulungu wanu limene anakulamulani, ndiponso chifukwa chakuti mwapita kukatumikira milungu ina ndi kuigwadira.+ Pamenepo, mkwiyo wa Yehova udzakuyakirani+ ndipo mudzatha mwamsanga padziko labwino limene iye anakupatsani.”+

  • Nehemiya 9:26
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 26 “Koma iwo anakhala osamvera+ ndipo anakupandukirani.+ Anapitiriza kufulatira chilamulo chanu,+ ndipo anapha aneneri anu+ amene anali kuwalimbikitsa kuti abwerere kwa inu.+ Iwo anapitiriza kuchita zinthu zikuluzikulu zosakulemekezani.+

  • Salimo 106:35
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 35 Iwo anayamba kusakanikirana ndi mitundu ina,+

      Ndi kuyamba kuphunzira zochita zawo.+

  • Amosi 5:7
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 7 Mukuweruza mopanda chilungamo,+ choncho moyo wakhala wowawa ndi wosautsa kwa anthu, pakuti inuyo mwakana chilungamo.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena