Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Esitere 3:12
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 12 Kenako anaitana alembi a mfumu+ m’mwezi woyamba, pa tsiku la 13 la mweziwo. Ndipo alembiwo analemba+ zonse zimene Hamani analamula masatarapi* a mfumu, abwanamkubwa a m’zigawo zosiyanasiyana+ za ufumuwo ndi akalonga a anthu osiyanasiyana m’chigawo chilichonse. Makalata amenewa anawalemba malinga ndi mmene anthu a m’chigawo chilichonse anali kulembera+ ndiponso m’chinenero chawo. Makalatawa anawalemba m’dzina+ la Mfumu Ahasiwero ndipo anawadinda ndi mphete yake yodindira.+

  • Esitere 8:9
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 9 Choncho anaitana alembi+ a mfumu pa nthawi imeneyo, m’mwezi wachitatu umene ndi mwezi wa Sivani,* pa tsiku la 23 la mweziwo. Iwo analemba makalatawo mogwirizana ndi zimene Moredekai ananena. Makalatawo anali opita kwa Ayuda, masatarapi,*+ abwanamkubwa ndi akalonga a m’zigawo zonse kuchokera ku Indiya kukafika ku Itiyopiya, zigawo 127.+ Chigawo chilichonse anachilembera makalata amenewa malinga ndi mmene anthu a m’chigawocho anali kulembera+ ndiponso m’chinenero chawo.+ Nawonso Ayuda anawalembera malinga ndi mmene iwo anali kulembera ndiponso m’chinenero chawo.+

  • Danieli 4:1
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 4 “Uwu ndi uthenga wochokera kwa ine mfumu Nebukadinezara wopita kwa anthu a mitundu yosiyanasiyana, olankhula zinenero zosiyanasiyana amene akukhala padziko lonse lapansi:+ Mukhale ndi mtendere wochuluka.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena