31 “‘Phokoso lidzamveka kumalekezero a dziko lapansi, pakuti Yehova akufuna kuimba mlandu mitundu ya anthu.+ Iye mwini adzalimbana ndi anthu onse powaweruza.+ Anthu oipa adzawapha ndi lupanga,’+ watero Yehova.
2 Inu mapiri, imvani mlandu umene Yehova ali nawo pa anthu ake. Inu matanthwe okhazikika, tamverani. Mvetserani inu maziko a dziko lapansi,+ pakuti Yehova ali ndi mlandu ndi anthu ake. Iye azenga mlandu Aisiraeli, kuti:+