-
Yeremiya 30:10Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
10 “Koma iwe Yakobo mtumiki wanga usachite mantha, iwe Isiraeli usagwidwe ndi mantha,”+ watero Yehova. “Pakuti ine ndikukupulumutsa kuchokera kutali ndipo ndikupulumutsanso ana ako kuchokera kudziko limene anatengedwa kukakhala akapolo.+ Yakobo adzabwerera ndipo adzakhala mosatekeseka komanso mopanda zosokoneza. Sipadzakhala womuopsa.”+
-
-
Yeremiya 33:9Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
9 Mzindawu udzakhala ndi dzina limene lidzandikondweretsa,+ dzina lochititsa kuti nditamandidwe ndi kulandira ulemerero pakati pa mitundu yonse ya padziko lapansi imene idzamva za zinthu zabwino zimene ndikuwachitira.+ Anthu a mitundu inawo adzachita mantha+ ndi kunjenjemera+ chifukwa cha zinthu zabwino ndi mtendere wonse umene ndikubweretsa pamzindawu.’”+
-