11 M’tsiku limenelo, Yehova adzaperekanso dzanja lake kachiwiri+ kuti atenge anthu ake otsala kuchokera ku Asuri,+ ku Iguputo,+ ku Patirosi,+ ku Kusi,+ ku Elamu,+ ku Sinara,+ ku Hamati ndi m’zilumba za m’nyanja.+
12 Ndiyeno Zerubabele+ mwana wa Salatiyeli ndi Yoswa mwana wa Yehozadaki+ mkulu wa ansembe, ndiponso anthu ena onse anayamba kumvetsera mawu a Yehova Mulungu wawo+ ndi a mneneri Hagai,+ chifukwa Yehova Mulungu wawo anamutuma. Pamenepo anthuwo anayamba kuchita mantha chifukwa cha Yehova.+