30 “‘Chotero ine ndidzaweruza aliyense wa inu malinga ndi njira zake,+ inu a nyumba ya Isiraeli,’ watero Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa.+ ‘Lapani ndi kusiya zolakwa zanu zonse+ ndipo musalole kuti chilichonse chizikupunthwitsani ndi kukulakwitsani.+
27 Pakuti Mwana wa munthu adzabwera ndithu mu ulemerero wa Atate wake limodzi ndi angelo ake. Pa nthawi imeneyo adzapatsa aliyense mphoto malinga ndi makhalidwe ake.+