Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Ekisodo 29:9
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 9 Ndiyeno Aroni ndi ana akewo uwamange malamba a pamimba. Ana akewo uwakulunge mipango kumutu kwawo ndipo unsembe udzakhala wawo. Limeneli ndi lamulo langa mpaka kalekale.+ Choncho upatse Aroni ndi ana ake mphamvu. +

  • Levitiko 16:11
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 11 “Choncho Aroni azipereka ng’ombe yamphongo ya nsembe yake yamachimo, kuti aphimbe machimo ake ndi a nyumba yake. Akatero azipha ng’ombe ya nsembe yake yamachimoyo.+

  • Aheberi 7:27
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 27 Iye safunikira kupereka tsiku ndi tsiku+ nsembe za machimo ake choyamba,+ kenako za anthu ena, monga mmene amachitira akulu a ansembe.+ (Iye anachita zimenezi kamodzi+ kokha pamene anadzipereka yekha nsembe.+ Nsembe imene anapereka motereyi ithandiza anthu mpaka muyaya.)

  • Aheberi 7:28
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 28 Chilamulo chimaika amuna okhala ndi zofooka+ kukhala akulu a ansembe.+ Koma mawu a lumbiro+ amene ananenedwa pambuyo pa Chilamulo anaika Mwana, amene anakhala wangwiro+ kosatha.

  • Aheberi 9:7
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 7 Koma m’chipinda chachiwiricho, mkulu wa ansembe yekha ndiye anali kulowamo kamodzi pa chaka,+ ndipo sanali kulowamo popanda kutenga magazi.+ Magaziwo anali kuwapereka chifukwa cha iye mwini,+ komanso chifukwa cha machimo a anthu amene anachita mosadziwa.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena