Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Levitiko 16:34
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 34 Limeneli likhale lamulo kwa inu mpaka kalekale,+ kuti machimo onse a Aisiraeli aziphimbidwa kamodzi pa chaka.”+

      Choncho iye anachita mogwirizana ndi zimene Yehova analamula Mose.

  • Aheberi 9:12
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 12 Iye analowa mʼmalo oyera ndi magazi ake,+ osati ndi magazi a mbuzi kapena a ngʼombe zazingʼono zamphongo. Analowa kamodzi kokha mʼmalo oyerawo ndipo anatipulumutsa kwamuyaya.+

  • Aheberi 9:24-26
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 24 Khristu sanalowe mʼmalo oyera opangidwa ndi manja a anthu,+ amene ndi chithunzi cha malo enieniwo,+ koma analowa kumwamba kwenikweniko.+ Panopa iye ali kumwamba kuti azionekera pamaso pa Mulungu mʼmalo mwa ifeyo.+ 25 Iye sanapite kumwambako kuti azikadzipereka nsembe mobwerezabwereza, ngati mmene mkulu wa ansembe amachitira. Paja mkulu wa ansembe amalowa mʼmalo oyera chaka ndi chaka+ atatenga magazi a nyama, osati ake. 26 Zikanatero, akanavutika mobwerezabwereza kuyambira pamene dziko linakhazikitsidwa. Koma tsopano iye waonekera kamodzi kokha pamapeto a nthawi* ino kuti achotse uchimo kudzera mu nsembe yake.+

  • Aheberi 10:10
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 10 Tayeretsedwa ndi “chifuniro” chimenecho,+ kudzera mʼthupi la Yesu Khristu limene analipereka nsembe kamodzi kokha.+

  • 1 Yohane 2:1, 2
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 2 Ana anga okondedwa, ndikukulemberani zinthu izi kuti musachite tchimo. Komabe, wina akachita tchimo, tili ndi wotithandiza wolungama,+ Yesu Khristu,+ amene ali ndi Atate. 2 Iye anakhala nsembe yophimba+ machimo athu.*+ Osati athu okha, komanso a dziko lonse lapansi.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena