Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Numeri 10:10
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 10 Komanso pa nthawi ya zisangalalo+ zanu, monga pa zikondwerero+ zanu ndi kumayambiriro kwa miyezi, muziliza malipenga popereka nsembe zanu zopsereza+ ndi zamgwirizano.+ Kulira kwa malipengawo kudzachititsa kuti Mulungu akukumbukireni. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.”+

  • 1 Mbiri 23:31
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 31 Ankathandizanso pa nthawi iliyonse yopereka nsembe zopsereza kwa Yehova pa Masabata,+ pa masiku amene mwezi watsopano waoneka+ ndi pa nthawi ya zikondwerero.+ Ankachita zimenezi nthawi zonse pamaso pa Yehova, malinga ndi ziwerengero zake zogwirizana ndi malamulo ake.

  • 2 Mbiri 2:4
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 4 Ine ndikumanga nyumba ya dzina la Yehova Mulungu wanga kuti ikhale yopatulika kwa iye. Ndikufuna kuti ndiziperekamo nsembe za mafuta onunkhira pamaso pake+ ndiponso kuti nthawi zonse muzikhala mkate wosanjikiza.*+ Ndiziperekamonso nsembe zopsereza mʼmawa ndi madzulo,+ pa Masabata,+ masiku amene mwezi watsopano waoneka+ ndi pa nthawi ya zikondwerero+ za Yehova Mulungu wathu. Aisiraeli afunika azichita zimenezi mpaka kalekale.

  • Nehemiya 10:32, 33
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 32 Kuwonjezera pamenepo, tinalonjeza kuti chaka chilichonse aliyense azipereka ndalama zasiliva zolemera magalamu 4* kuti akazigwiritse ntchito pa utumiki wapanyumba* ya Mulungu wathu.+ 33 Akazigwiritsenso ntchito pokonza mkate wosanjikiza,*+ nsembe yambewu+ yoperekedwa nthawi zonse, nsembe yopsereza yoperekedwa nthawi zonse pa Masabata+ ndi pa masiku amene mwezi watsopano waoneka,+ madyerero a pa nthawi yoikidwiratu,+ zinthu zopatulika, nsembe yamachimo+ yophimba machimo a Isiraeli komanso pa ntchito zonse zapanyumba ya Mulungu wathu.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena