-
Numeri 28:3-8Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
3 Uwauze kuti, ‘Nsembe yowotcha pamoto imene muzipereka kwa Yehova ndi iyi: tsiku lililonse muzipereka nsembe yopsereza ya ana a nkhosa awiri amphongo, achaka chimodzi komanso opanda chilema.+ 4 Mwana wa nkhosa mmodzi wamphongo muzimupereka nsembe mʼmamawa. Ndipo mwana wa nkhosa wamphongo winayo, muzimupereka nsembe madzulo kuli kachisisira.*+ 5 Muzipereka nsembezi limodzi ndi ufa wosalala wokwana gawo limodzi mwa magawo 10 a muyezo wa efa,* kuti ikhale nsembe yambewu. Ufawo muziuthira mafuta oyenga bwino kwambiri okwana gawo limodzi mwa magawo 4 a muyezo wa hini.*+ 6 Imeneyi ndi nsembe yopsereza+ ya tsiku ndi tsiku imene ndinakulamulani kuphiri la Sinai. Ndinakulamulani kuti muziipereka kwa Yehova kuti ikhale nsembe yakafungo kosangalatsa,* yowotcha pamoto. 7 Muziipereka pamodzi ndi nsembe yachakumwa chokwana gawo limodzi mwa magawo 4 a muyezo wa hini. Pa mwana wa nkhosa wamphongo aliyense+ muzipereka nsembe yachakumwa. Muzithirira Yehova nsembe yachakumwa choledzeretsa mʼmalo oyera. 8 Mwana wa nkhosa wamphongo winayo muzimupereka nsembe madzulo kuli kachisisira.* Muzimupereka limodzi ndi nsembe yambewu ndiponso yachakumwa, mofanana ndi nsembe ya mʼmamawa ija. Izikhala nsembe yowotcha pamoto yakafungo kosangalatsa* kwa Yehova.+
-