-
Yesaya 20:3, 4Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
3 Kenako Yehova anati: “Mtumiki wanga Yesaya wayenda maliseche ndiponso wopanda nsapato kwa zaka zitatu, kuti akhale chizindikiro+ ndi chenjezo kwa Iguputo+ ndi Itiyopiya.+ 4 Mofanana ndi zimenezi, mfumu ya Asuri idzagwira gulu la anthu ku Iguputo+ ndi ku Itiyopiya nʼkupita nawo ku ukapolo kudziko lina. Idzagwira anyamata ndi amuna achikulire, ali opanda zovala ndi opanda nsapato, ndiponso matako awo ali pamtunda moti Iguputo adzachititsidwa manyazi.
-
-
Yeremiya 46:25, 26Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
25 Yehova wa magulu ankhondo akumwamba, Mulungu wa Isiraeli, wanena kuti: ‘Tsopano ndilanga Amoni+ wa ku No,*+ Farao, Iguputo pamodzi ndi milungu yake+ ndi mafumu ake. Inde ndilanga Farao ndi onse amene amamukhulupirira.’+
26 ‘Ndidzapereka anthu a ku Iguputo mʼmanja mwa anthu amene akufuna moyo wawo, mʼmanja mwa Nebukadinezara* mfumu ya Babulo+ ndi mʼmanja mwa atumiki ake. Koma kenako anthu adzakhalanso mʼdzikolo ngati mmene zinalili kale,’ akutero Yehova.+
-