Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g88 3/8 tsamba 31
  • Kumaliyang’ana Dziko

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kumaliyang’ana Dziko
  • Galamukani!—1988
  • Timitu
  • Nkhani Yofanana
  • AIDS Iwopsyeza Asia
  • “Malonda a Anyani”
  • Akazi Amakhala ndi Moyo Wotalikirako
  • Opanda Nyumba Kulikonse
  • Anthu Miyandamiyanda Padziko Lonse Akuyamikira Baibulo la New World Translation
    Nsanja ya Olonda—2001
  • Chochitika Chosaiŵalika kwa Okonda Mawu a Mulungu
    Nsanja ya Olonda—1999
  • AIDS—Imfa Yake Yowopsa pa Ana
    Galamukani!—1991
  • Kodi Ndani Amene Ali Pangozi?
    Galamukani!—1986
Galamukani!—1988
g88 3/8 tsamba 31

Kumaliyang’ana Dziko

AIDS Iwopsyeza Asia

Nthenda yakupha ya AIDS ikuwopsyeza Aisa ndi mliri, inachenjeza tero WHO (World Health Organization). “Ngati tilola AIDS kufalikira mu Asia, ndiko kuti tidzakhala ndi vuto kwenikweni,” anatero mtsogoleri wa zaumoyo wa WHO Halfdan Mahler, kulingana ndi gulu lofalitsa nkhani ya mitundu yonse. Ngakhale kuti North ndi South America tsopano ziri ndi chiŵerengero chapamwamba cha matenda ochitiridwa ripoti a AIDS ndipo Asia chaching’ono, WHO ikuwopa kuti pamene kachirombo kodzetsa imfa kafalikira ku mitundu yokhala ndi chiŵerengero chokulira cha anthu ku Asia, boma silidzakhala lokhoza kufufuza kakulidwe kake. “Ndiri ndi mantha kuti muli ndi malo kaamba ka tsoka lokulira,” anatero Mahler. “Ndiridi ndi mantha ponena za chimenecho.”

“Malonda a Anyani”

Ngati munali m’malonda a coconut, kodi ndani yemwe mukalemba ntchito monga wotola? Mu dera la kumpoto la Surati Thani, Thailand, kampani imodzi inalowetsa ntchito chifupifupi anyani 800 kuchita ntchitoyo. Pansi pa mphatso ya $4,000 (U.S.) yoperekedwa ndi banja lachifumu la ku Thai, anyani akupatsidwa chiphunzitso chaluso cha mmene angatolere macoconuts m’mitengo. Komabe, “palibe nyani wachikulire aliyense yemwe angachite chimenecho,” inachitira ripoti tero The Economist. Ena alibe chifuno kaamba ka ntchito, monga mmene ziriri zowona ndi ‘okhala ndi nsidze zoyera’ kusiyanasiyana kwawo—iwo kaŵirikaŵiri amatsimikizira kukhala aulesi kwambiri. Mosiyanako, nyani wokhala ndi chizoloŵezi cha ntchito angakhoze kutola unyinji wa macoconut zikwi zingapo tsiku lirilonse, inadziŵitsa tero The Economist. Ngati akanapatsidwa malipiro olingana ndi ntchito yake, iye akapeza kuposa mtumiki wa boma wapakati mu boma la Thai. Mosasamala kanthu ndi umoyo wa ntchito wa kokha chifupifupi zaka zisanu, iwo ali oyenerera bwino lomwe kukhala chuma chosungidwa. Iwo amawononga chifupifupi $40 kuti aphunzitsidwe.

Akazi Amakhala ndi Moyo Wotalikirako

Chakhala chikudziŵika kwa nthaŵi yaitali kuti akazi amakhala kwa nthaŵi yaitali kuposa amuna. Kufufuza kwa posachedwapa kwasonyeza kuti, ngakhale mu umoyo wa kubadwa kusanachitike, imfa za m’mimba, pa avereji, zakhala zochulukira 50 peresenti pakati pa makanda osabadwa achimuna kuposa pakati pa makanda osabadwa achikazi. Tsopano, nkhani yofalitsidwa mu British Medical Journal yatsimikizira kuti akazi amakhalabe kwa nthaŵi yaitali kuposa amuna. Alan Silman, mkonzi wa nkhaniyo ndi mphunzitsi pa London Hospital Medical College, wadziŵitsa kuti ngakhale m’maiko otukuka kumene, akazi amachitira avereji zaka chifupifupi zisanu ndi chimodzi zowonjezereka za kuyembekezeredwa kwa umoyo kuposa mmene amuna amachitira. Iye akusimba kuti mu England ndi Wales, gulu lachitatu la chiŵerengero chonse cha akazi a zaka 65 angayembekeze kupulumuka ku msinkhu wa zaka 80, kulinganizidwa ndi kokha aŵiri mu amuna asanu. Chochititsa? Akazi ali ndi chizoloŵezi cha kukhala ndi ngozi zochepera, amachezera adokotala awo kaŵirikaŵiri, ndipo mwinamwake chofunika koposa, amasuta mochepera. Kuwonjezerapo, uchidakwa uli wosafala pakati pa akazi kuposa pakati pa amuna. Komabe, kulingana ndi Mr. Silman, “pali kuwawa kobisika.” Zaka zowonjezereka zimene akazi amapulumuka ziri kaŵirikaŵiri za “mkhalidwe woipa,” zotsirizidwa mu kudzipatula kwa mayanjano ndi kusauka.

Opanda Nyumba Kulikonse

Munthu wachinayi aliyense padziko ali kaya wopanda nyumba kapena amakhala pansi pa “makoma owonongeka ndi a mkhalidwe wosakhala waumoyo wabwino.” Kufufuza kochitidwa ndi Mitundu Yogwirizana kunavumbula kuti chifupifupi anthu mamiliyoni 100 anakhoza kugona m’makwalala, pansi pa maulalo, m’zipata, kapena pa malo osiidwa. Maperesenti makumi aŵiri a anthu oterewa ali achichepere mu Latin America. Mu mizinda ya mu Africa, kufika ku maperesenti 80 a nzika zonse amakhala m’nyumba zauve. United States iri ndi anthu opanda nyumba mamiliyoni 2.5, ndipo mu Great Britain chiŵerengero chiri chifupifupi 250,000.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena