Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 6/08 tsamba 4
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2008
  • Nkhani Yofanana
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2009
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2009
  • Zimene Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2010
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2007
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2008
km 6/08 tsamba 4

Zomwe Munganene Pogawira Magazini

Nsanja ya Olonda June 1

“Kodi mukuganiza kuti Mulungu amavomereza zipembedzo zonse? [Yembekezani ayankhe.] Taonani zimene Mulungu ananena Aisiraeli atatengera miyambo ya zipembedzo za mitundu ina. [Werengani Ezekieli 6:6.] Nkhani iyi ikuyankha funso lakuti: ‘Kodi Mulungu Amavomereza Kulambira Kulikonse?’” M’sonyezeni nkhani yomwe yayambira patsamba 9.

Galamukani! June

“Mosakayikira, mungavomereze kuti zimakhala zovuta kwa mwana ndiponso makolo ake, makamaka mwanayo akamasinkhuka. Kodi mukuganiza kuti malangizo awa angathandize makolo kulera bwino ana awo? [Werengani Yakobe 1:19. Ndiyeno, yembekezani ayankhe.] Musangalala kwambiri ndi mfundo zabwino zochokera m’Baibulo zomwe zili m’magazini iyi.”

Nsanja ya Olonda July 1

“Tonsefe tinavutikapo ndi chisoni munthu amene tinali kumukonda atamwalira. Panthawi yotereyi, kodi mukuganiza kuti Baibulo lingatithandize? [Yembekezani ayankhe. Kenako werengani Salmo 55:22.] Magazini iyi ikufotokoza mfundo za m’Baibulo zimene zingatilimbikitse.”

Galamukani! July

“Anthu a pabanja akukumana ndi mavuto ochuluka ndipo ambiri akumasudzulana. Kodi mukuganiza kuti kutsatira malangizo awa kungathandize kuti ukwati uziyenda bwino? [Werengani Miyambo 12:18. Kenako, yembekezani ayankhe.] Magazini iyi ili ndi mfundo za m’Baibulo zimene zingathandize anthu a pabanja kuti akhale ndi ukwati wolimba.”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena