Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 4/10 tsamba 1
  • Kopani Chidwi Pophunzitsa

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kopani Chidwi Pophunzitsa
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2010
  • Nkhani Yofanana
  • Kugwiritsa Ntchito Malemba Moyenerera
    Pindulani ndi Sukulu ya Utumiki wa Mulungu
  • Kodi Mumadalira Mawu a Mulungu?
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2007
  • Gwiritsani Ntchito Mwaluso “Lupanga la Mzimu”
    Nsanja ya Olonda—2010
  • Mmene Tingakopere Ena
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2001
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2010
km 4/10 tsamba 1

Kopani Chidwi Pophunzitsa

1. Kodi kugwiritsa ntchito Mawu a Mulungu mokopa mu utumiki kumaphatikizapo chiyani?

1 Aphunzitsi aluso, monga mtumwi Paulo, amadziwa kuti ‘kulondoloza bwino mawu a choonadi’ kumafuna zambiri osati kungotchula mawu okha a m’Malemba Oyera. (2 Tim. 2:15) Pogwiritsa ntchito Mawu a Mulungu, kodi tingatani kuti ‘tikope’ chidwi pophunzitsa?—Mac. 28:23.

2. Kodi mungatani kuti muthandize anthu kulemekeza Mawu a Mulungu?

2 Sonyezani Omvera Anu Zimene Mawu a Mulungu Amanena: Choyamba, awerengereni zimene Baibulo likunena n’cholinga choti azililemekeza kuti ndi Mawu a Mulungu. Tikamadalira kwambiri Mawu a Mulungu, nawonso omvera athu amamvetsera mwachidwi tikamawerenga malemba. (Aheb. 4:12) Tikamakambirana ndi munthu Mawu a Mulungu, tinganene kuti: “Ndikuona kuti kuyendera maganizo a Mulungu pankhaniyi n’kothandiza. Taonani zimene Mawu ake akunena.” Ngati n’kotheka, muziyesetsa kuwerenga Baibulo kuti omvera anu aone zimene Mawu a Mulungu akunena.

3. Mukawerenga lemba, kodi mungatani kuti muthandize omvera anu kumvetsa mfundo ya lembalo?

3 Chachiwiri, fotokozani lemba limene mwawerenga. Anthu ambiri akangowerenga vesi koyamba zimawavuta kumvetsa tanthauzo lake. Choncho, tiyenera kufotokoza mfundo ya lembalo. (Luka 24:26, 27) Tsindikani mawu ofunika palembalo amene akugwirizana ndi zimene mukukambirana. Kuwafunsa funso kungathandizenso kuti mudziwe ngati omvera anu amvetsa mfundo ya lembalo.—Miy. 20:5; Mac. 8:30.

4. Kodi ndi mfundo yomaliza iti imene ingathandize kuti tikope chidwi cha anthu pophunzitsa?

4 Fotokozerani Malemba: Chachitatu, yesetsani kuti muwafike pamtima omvera anu. Thandizani eninyumba kuti aone mmene lembalo lingawathandizire paokha. Kufotokozera malemba kungathandize munthu kusintha maganizo ake. (Mac. 17:2-4; 19:8) Mwachitsanzo, mukawerenga Salmo 83:18, fotokozani mmene kudziwa dzina la munthu winawake kulili kofunika kuti mukhale naye paubwenzi wabwino. Ndiyeno, m’funseni kuti, “Kodi mukuganiza kuti kudziwa dzina la Mulungu kungathandize kuti mapemphero anu azikhala ogwira mtima?” Kugwirizanitsa lembalo ndi moyo wa munthuyo, kungamuthandize kuona mmene angagwiritsire ntchito mfundozo pamoyo wake. Kukopa chidwi cha anthu pophunzitsa mwa kugwiritsa ntchito Mawu a Mulungu kumapangitsa anthu oona mtima kuyamba kulambira Yehova, yemwe ndi Mulungu woona ndiponso wamoyo.—Yer. 10:10.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena