Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 2/13 tsamba 3
  • Kodi Inunso Muyenera Kutuluka mu Utumiki?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Inunso Muyenera Kutuluka mu Utumiki?
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2013
  • Nkhani Yofanana
  • Ulaliki wa Mumsewu Wopindulitsa
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2011
  • Lalikirani Uthenga Wabwino Paliponse
    Utumiki Wathu wa Ufumu—1996
  • Muzigwiritsa Ntchito Bwino Nthawi Mukakhala mu Utumiki
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2015
  • Kupeza Okondwerera Kupyolera mu Umboni wa m’Khwalala Wogwira Mtima
    Utumiki Wathu wa Ufumu—1994
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2013
km 2/13 tsamba 3

Kodi Inunso Muyenera Kutuluka mu Utumiki?

Ofalitsa ena ali ndi nthawi imene anazolowera kutuluka mu utumiki wakumunda, mwina 12 koloko masana. M’pomveka kuti ofalitsa ena, malinga ndi mmene zinthu zilili pa moyo wawo, amafunika kutuluka mu utumiki pa nthawi inayake yokhazikika. Koma kodi inunso mumatuluka mu utumiki chabe chifukwa chakuti ofalitsa ena akutuluka, kapena chifukwa choti ofalitsa a m’dera lanu anazolowera kutuluka mu utumiki pa nthawi inayake? N’zotheka kupitiriza kulalikira kwa mphindi zingapo, ngakhale pamene anzanu akutuluka mu utumiki. Mwina mukhoza kuyamba kulalikira m’malo amene mumapezeka anthu ambiri, monga mumsewu. Pobwerera kunyumba kwanu, mungathenso kupita ku maulendo anu obwereza. Taganizirani mmene mungathandizire munthu wachidwi, ngakhale mmodzi yekha, yemwe mungamuyenderenso n’kumupeza pakhomo. Kapena taganizirani mmene mungathandizire anthu amene mwakumana nawo mumsewu n’kuwagawira magazini. Ngati ifeyo tingapitirize kulalikira kwa mphindi zingapo pamene ena akutuluka mu utumiki, ndiye kuti tikuwonjezerera “nsembe” yathu yotamanda Mulungu.—Aheb. 13:15.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena