Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb16 March tsamba 8
  • Kuwonjezera Luso Lathu mu Utumiki—Kukonza Ulaliki Wanuwanu wa Magazini

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kuwonjezera Luso Lathu mu Utumiki—Kukonza Ulaliki Wanuwanu wa Magazini
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2016
  • Nkhani Yofanana
  • Mmene Mungakonzekerere Kugawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2006
  • Mmene Tingagwiritsire Ntchito Zitsanzo za Maulaliki
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2005
  • Gawirani Magazini Amene Amachitira Umboni Choonadi
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2007
  • Zitsanzo za Ulaliki
    Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2018
Onani Zambiri
Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2016
mwb16 March tsamba 8

KUWONJEZERA LUSO LATHU MU UTUMIKI

Kukonza Ulaliki Wanuwanu wa Magazini

Losindikizidwa
Amboni za Yehova akukambirana ndi munthu nkhani ya m’magazini

N’CHIFUKWA CHIYANI TIYENERA KUCHITA ZIMENEZI?: Zitsanzo za ulaliki zomwe zimakhala mu Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu ndi zothandiza, koma sitiyenera kuloweza chifukwa ndi zongotithandiza kudziwa zimene tinganene. Tiyenera kukonzekera m’mawu athuathu. Tingagwiritsenso ntchito ulaliki wina kapena nkhani ina yogwirizana ndi gawo lathu. Choncho tikawerenga magazini, kuona zitsanzo za ulaliki komanso kuonera vidiyo, tikhoza kugwiritsa ntchito mfundo zotsatirazi kuti tikonze ulaliki wathu.

KODI TINGACHITE BWANJI ZIMENEZI?

Dzifunseni kuti, ‘Kodi ineyo ndingakonde kugwiritsa ntchito chimodzi mwa zitsanzo za ulalikizi?’

INDE

  • Chikonzekereni m’mawu anuanu. Pambuyo popereka moni fotokozani cholinga chanu. (Mwachitsanzo, munganene kuti: “Ndabwera kuti . . .”)

  • Ganizirani zimene munganene pambuyo poti mwafunsa funso, pambuyo poti mwawerenga lemba komanso pambuyo poti mwapereka magazini. (Mwachitsanzo, pofuna kutchula lemba munganene kuti: “Yankho la funso limeneli tingalipeze palemba ili.”)

AYI

  • Sankhani nkhani imene yakusangalatsani komanso imene anthu a m’gawo lanu angasangalale nayo

  • Ganizirani funso limene lingachititse munthuyo kufotokoza maganizo ake. Koma funsolo lisakhale lochititsa manyazi. (Mwachitsanzo, mungasankhe funso limodzi pa mafunso amene ali patsamba 2 la magaziniyo.)

  • Sankhani lemba loti mukawerenge. (Ngati ndi Galamukani! mungasankhe kukawerenga lemba kapena ayi chifukwa magaziniwa amalembera anthu amene sadziwa bwino Baibulo komanso mwina amakayikira zochita za zipembedzo.)

  • Konzani mawu amene mungauze munthu amene mukumulalikirayo, omuthandiza kuona mmene angapindulire akawerenga magaziniyo

KAYA MWASANKHA INDE KAPENA AYI:

  • Konzani funso loti mudzayankhe pa ulendo wobwereza

  • Lembani mfundo zokuthandizani kukumbukira zimene mudzanene

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena