Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb23 January tsamba 5
  • Muzikhulupirira Kwambiri Mawu a Mulungu

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Muzikhulupirira Kwambiri Mawu a Mulungu
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2023
  • Nkhani Yofanana
  • Zosankha Zomwe Zimasonyeza Kuti Timadalira Yehova
    Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2023
  • Muziwerenga Baibulo Tsiku Lililonse Komanso Muzifunafuna Nzeru
    Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2023
  • Mupeze Mayankho a Mafunso Awa
    Pulogalamu ya Msonkhano Wadera Wokhala ndi Woyang’anira Dera wa 2025-2026
  • Mupeze Mayankho a Mafunso Awa
    Pulogalamu ya Msonkhano Wadera Wokhala ndi Woimira Nthambi wa 2025-202
Onani Zambiri
Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2023
mwb23 January tsamba 5
Zithunzi za mlongo wachinyamata akuwerenga komanso kuphunzira Baibulo: 1. Akupanga tchati cha anthu otchulidwa m’Baibulo. 2. Akuwerenga “Baibulo la Dziko Latsopano” lachingelezi la Study Edition pa jw.org. 3. Akufufuza pogwiritsa ntchito mapu a malo otchulidwa m’Baibulo. 4. Akujambula chithunzi cha mkulu wa ansembe ndipo akuika mayina pa chovala cha wansembeyo.

MOYO WATHU WACHIKHRISTU

Muzikhulupirira Kwambiri Mawu a Mulungu

Mawu a Mulungu akhoza kusintha moyo wathu. (Ahe 4:12) Komabe kuti malangizo komanso uphungu wake uzitithandiza, tiyenera kukhulupirira kuti ndi “mawu a Mulungu.” (1At 2:13) Kodi tingatani kuti tizikhulupirira kwambiri Baibulo?

Tsiku lililonse tiziwerenga kachigawo kenakake ka Baibulo. Tikamawerenga, tizifufuza umboni woti Yehova ndi amene analilemba. Mwachitsanzo, fufuzani malangizo anzeru omwe amapezeka m’buku la Miyambo, ndipo onani mmene amatithandiziranso ifeyo masiku ano.​—Miy 13:20; 14:30.

Yambani kuphunzira zokhudza Baibulo. Muzipeza maumboni otsimikizira kuti Baibulo ndi buku louziridwa. Mu Buku la Mboni za Yehova Lofufuzira Nkhani, pitani pamene alemba kuti “Baibulo” kenako “Kuuziridwa ndi Mulungu.” Mungalimbitsenso chikhulupiriro chanu chakuti uthenga wa m’Baibulo sunasinthe pofufuza mfundo zimene zili mu Nsanja ya Olonda Na. 4 2016.

ONERANI VIDIYO YAKUTI N’CHIFUKWA CHIYANI TIMAKHULUPIRIRA . . . MAWU A MULUNGU?, KENAKO YANKHANI MAFUNSO OTSATIRAWA:

  • Kodi zomwe zinapezeka pa khoma la kachisi ku Kanaki ku Iguputo, zimatsimikizira bwanji kuti Baibulo limanena zoona?

  • Kodi timadziwa bwanji kuti uthenga wa m’Baibulo sunasinthe?

  • Kodi mfundo yakuti Baibulo lapulumuka zambiri imakutsimikizirani bwanji kuti ndi Mawudi a Mulungu?​—Werengani Yesaya 40:8

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena