Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 3/02 tsamba 8
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
  • Utumiki wathu wa Ufumu—2002
  • Nkhani Yofanana
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2007
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2008
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2006
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2004
Onani Zambiri
Utumiki wathu wa Ufumu—2002
km 3/02 tsamba 8

Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini

Nsanja ya Olonda Mar. 15

“Kodi mukuvomereza kuti ulamuliro wolungama ungasandutse dzikoli kukhala malo abwino kwa anthu kukhalamo? [Yembekezani ayankhe.] Taonani zimene Baibulo likulonjeza. [Ŵerengani Salmo 37:11.] Tikhoza kusangalala ndi mtendere umenewu, umene udzakhalepo mu ulamuliro wa Mtsogoleri wangwiro amene amutchula mu nkhani izi.”

Galamukani! Apr. 8

“Zivomezi zingaphe anthu ochuluka komanso zingawononge zinthu zambiri zedi. Nthaŵi zambiri anthu opulumuka pangozi zimenezi amakhala opanda nyumba. Amakhala alibiretu zoti n’kuwathandiza kukhalanso ndi moyo wabwino. Galamukani! iyi ikusonyeza zimene anthu okhudzidwa ndi ngozi zoterezi achita kuti apirire mavuto amene amabwera chifukwa cha chivomezi. Ikusonyezanso kuti ulosi wofunika kwambiri m’Baibulo umanena za zivomezi.”

Nsanja ya Olonda Apr. 1

“Ndikufuna ndikuuzeni mawu a m’Baibulo olimbikitsa kwambiri aŵa. [Ŵerengani Mateyu 22:37.] Kodi mukuganiza kuti mawu ameneŵa akutanthauza chiyani? [Yembekezani ayankhe.] Taonani nkhani iyi yakuti, ‘Funani Mulungu ndi Mtima ndi Maganizo Anu.’ Kodi chikhulupiriro chenicheni n’chofunika kukhudza mtima wokha, kapena ndi maganizo omwe? Yankho lake n’lothandiza kwambiri.”

Galamukani! Apr. 8

“Monga mukudziŵa, masiku ano kusamalira banja si ntchito yamaseŵera, komanso kukhala mayi n’chintchito chovuta. Galamukani! iyi ili ndi malangizo abwino pankhani iyi yamutu wakuti ‘Kodi Kukhala Mayi Kumalira Ukatswiri?’ Ndikusiyirani magazini imeneyi.”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena